Bwanji Za Mankhwala, Zoledzeretsa, Ndi Chiwerewere?
"Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa..."
(Aroma 6:23)
Tiyeni tinene zoonadi. Zirombo zoopsya kumwa zoledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere ziri nkuopsyeza ndiponso kuononga chimene Mulungu anachilenga kukhala chokoma ndiponso chabwino. Monga mchitidwe wa Octopus wamphamvuyo, izi zimakoka ang'ono komanso aakulu ndi kuwafumbatira.
Anthu ambiri amakakamizidwa pambali iliyonse ndi zokhumba zao, monga manyuzi pepala komanso ndi kuitanira kwa television. Maso ndi makutu zimalunjika kumene kuli zosokoneza zokhazokha zomwe zotsatira zake ndi kukhala ndi moyo wa uzimu komanso wa kuthupi wobwerera m'mbuyo. Temberero la chakumwa choledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere zaleka chitsanzo chokoma cha m’midzi yathu popanda kuongoledwa ndipo ziri nkupita ku chionongeko.
Kodi nanga ndi mbadwo wokha wa ana womwe utsutsidwe? Ayi. Naonso makolo ambiri asiyanso chikhalidwe chokoma, natsata chikhalidwe choipa, machismo ambiri ochitidwa ndi ana ambiri lero, makolo awo amangowalekerera osadziwa kuti alikupanga ana awo kuti adzakhale zidakwa, ogwiritsa ntchito mankhwala osaloledwa, ndi osuta pakulephera iwo kudzudzula pa kumwa zoledzeletsa ndi kusuta.