Kulapa: Khomo la Chifundo

Wokondedwa Moyo'we: Kodi ukudziwa kuti wapezeka wochimwa ndi Mulungu Woyerayo, ndi kuti kwaikidwa kwa iwe kufa? Ngati munthu wochimwa afuna kuithawa imfa ya muyayayi ndi kupulumutsidwa ku nthawi zosatha, iye ayenera kulandira chifundo cha Mulungu'chi. Chifundo chimatiteteza ife pa chirmene tikadalandira. Komatu Mulungu samangoika chifundo chake pa anthu popanda choyenereza ayi, ngakhale kuti chipulumutso nchaulere, chopanda mtengo wake (chosagula) ndiponso chosati nkuchigwirira ntchito. Chotiyenereza chakuti Mulungu atipatse ife chifundo chake chipezeka mu liu limodzi lokha: Lapani.

Yohane Mbatizi anadza nalalikira Mau a Mulungu ndipo uthenga wake unali wokhweka, koma wamphamvu. "Lapani inu chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira" (Mateyu 3:2). Yesu, Mwana wa Mulungu, anayamba utumiki wake ndi uthenga womwewo, "Lapani pakuti ufumu wakumwamba wayandikira" (Mateyu 4:17). Kulapa ndicho chotiyenereza cha chipulumutso monga Mtumwi petro ananena, "Chifukwa chake lapani, bwererani kuti afafanizidwe machimoanu" (Machitidwe 3:19). Kulapa ndi khomo loyenera kutsegulidwa ngati chifundo chingaonjezedwe ndi chipulumutso kupatsidwa.

Mdziko lapansi lathuli muli unyinji wa anthu, bwenzi langawe, mnjira zambiri timasiyana wina ndi mnzake. Komabe pali mbali ina imene tonse pamodzi timagawana popanda wotsala. Mau a Mulungu amationetsera ife bwino mbali imeneyi pamene amati: "Pakuti ONSE anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu" (Aroma 3:23). Ndipo tamveraninso, "Palibe M'MODZI wolungama, inde palibe m'modzi" (Aroma 3:10). Mulungu ananena kupyolera mwa mneneri wake Yesaya ndi kuti, "Tonse tasochera ngati nkhosa, tonse tayenda yense mnjira ya mwini yekha" (Yesaya 53:6). Kodi ulikudziwa cholinga chenicheni cha malemba oyerawa? "ONSE anataika". "PALIBE wolungama". "ONSE anachimwa". Wokondedwa wowerenganu, kodi ichi sichili kukukhudzani? Mzimu wanu, mayo wanu ndi za Mulungu. Mwamuna kapena mkazi ngakhale mwana kapena wamkulu amene sazindikira Mulungu monga mwini wa moyo wake aneneyo ali mkusamvera ndi mtchimo. "Moyo wochimwawo ndiwo udzafa" (Ezekieli 18:4).

Machimo anu akulekanitsani inu ndi Mulungu. Mumamva kufunafuna mkati mwanu kotero kuti simungathe kukufotokoza ayi. Mungathe kuona ngati ndinu wotayika ndi kuti Mulungu sakumva. Chifukwa chake Mulungu achitchula, "Taonani mkono wa Yehova sufupika, kuti sungathe kupulumutsa; khutu lake silili logontha, kuti silingamve; koma zoipa zanu zakulekanitsani inu ndi Mulungu wanu; ndipo machimo anu abisa nkhope yake kwa inu kuti lye sakumva" (Yesaya 59:1-2). Ndiponso, "Mphotho yake ya uchimo ndi imfa" (Aroma 6:23). Pamene muli kulingilira za moyo wanu ndi machimo anu, lingiliraninso za Mulungu. Mulungu alibe tchimo, choncho lye ndi Woyera, wolungama ndi wolunjika. Mulungu amati tchimo liyenera kuweruzidwa. "Pakuti Mulungu adzaweruza mlandu wa zochita zonse, ndi zobisika zonse, kaya zabwino ngakhale zoipa" (Mlaliki 12:14). Pali phompho lalikulu loikika pakati pa inu ndi Mulungu, ndi imfa yamuyaya, pokhapokha titapeza njira yomwe ipyola phompholo ndi kukoka wochimwayo pa maso pa Mulungu Woyerayo (Luka 16:26). lnde ilipo njira, chilipo chiyembekezo chanu!

Nkhani yonse ya: Kulapa: Khomo la Chifundo

Pamene tiona kuti Mulungu anaika chiweruzo cha imfa chifukwa cha tchimo, lyenso ndi Mulungu wachikondi. "Mulungu ndiye chikondi" (1 Yohane 4:16). Mulungu akukondani, mnzanga, ngakhale mukukhala mu uchimo. Chikondi chake chidakukonzerani njira yoti mupulumutsidwe nayo (Yohane 3:16). Mulungu, wosanamayo, adzaika chiweruzo chake pa tchimo, ndipo ngati chilungamo chake sichidzakhala pa munthu, pomwepo iye adzafa. Chomwecho Mulungu safuna wina aliyense kuti ataike, anatuma Mwana wake Yesu kutitengera thonzo la uchimo kuti tikhale ndi moyo. Malemba akuti, "Chifukwa chake onani chifatso chake ndi kuuma mtima kwake kwa Mulungu" (Aroma 11:22). Ubwino wa Mulungu ndi wakuti apulumutse munthu koma chiweruzo chake chinkafuna chilango.

Yesu anadza ku dziko lapansi ndi cholinga chakuombola miyoyo yathu. Iye ndi Woyera ndi wopanda tchimo, Mwana-wa-Nkhosa wa Mulungu wopanda chilema. Chikondi cha Mulungu chapa ife chinaoanekera pamene lye anatenga machimo athu ndi kulakwa kwathu ndi mphotho yake ya imfa ndi kuziika izi pa Yesu. Taonani ubwino wake! Ndipo monga Yesu anamvera chifuniro cha Atate wake, lye analandira mphotho ya machimo athu. Yesu anakhala wochimwa m'malo mwathu ndi kukwaniritsa chiweruzo cha Mulungu. Iye anapachikidwa pa mtanda pa maora asanu ndi limodzi (6 hours) namva kuwawa ndi ululu kufikira mphotho yake ya machimo athu itaperekedwa, ndipo pamenepo Yesu anafa. Taonani kuuma mtima kwake kwa Mulungu!

Wokondedwa wowerenganu, kodi mukuona kuti Yesu anakuferani inu, ndi kuti lye anafa CHIFUKWA cha machimo anu? Kodi makamaka yemwe adapachika Yesu ndani? Kodi amene anakhudzidwa ndi akuluakulu a Ayuda, kapena Pilato kapena asilikari a Aroma okha? Petro mtumwi tsiku lina analalikira kwa chikhamu cha anthu zikwizikwi. Uthenga wake wa Petro unali woona: "lye (Yesu), anaperekedwa ndi chikhamu komanso ndi nzeru ya kudziwiratu ya Mulungi, INU munamtenga ndi manja anu oipawo munampachika ndi kumupha" (Machitidwe 2:23). Wokondedwa moyowe, yang'anani kwa Yesu yemwe anapachikidwa ndipo bvomerezani kulakwa kwanu ndi kuchita naye mu imfa yake!

Kulapa koonadi kumayambira makamaka pa mfundo imeneyi, pamene musunga mu mtima mwanu za malo owopsyawo ndi zomwe zinachitikazo. Ndi mphamvu ya Mzimu wa Mulungu mudzazindikira kuti mukanayenera kufa munali inu osati Yesu ayi. Koma Yesu anatenga malo anu! Ngati inu muzindikira ichi mumtima mwanu, kudzakubweretserani chisoni ndi kuti tchimo simudzalifunanso ayi. Pakulingirira kuti wina adakonzera wina imfa ndi chinthudi chochititsa mantha, makamaka kuti lye anali Mwana weniweni wa Mulungu. Miyoyo yomwe imagwira masomphenya awa imalapa ndi kubvomereza machimo awo. Ndi monga momwe tilingirira za chiweruzo cha Mulungu chokhuthulidwa pa Yesu ndipo pakuchidziwa ichi tidayenera kulira ndi ife omwe tidayenera imfa, "Mulungu mundichitire chifundo ine wochimwa" (Luka 18:13). lzi ndi ntchito zoyamba za kulapa. Ngati kulapaku kupitirira, kumakwaniritsa pa kusiyiratu njira zathu zoyamba za uchimozo, ndi kutembenukira ku njira za Mulungu. Munthu yemwe watsukidwa ndi kuyeretsedwa kuchokera ku njira zake zoipazo, iye adzazifulatira izo ndi kutembenukira ku zinthu zakumwamba. ichi mwachidule ndi njira yolapa yomwe imachitika ndi Mulungu mu mitima ya onse akudza kwa lye. Pokhapokha munthu atalapadi, ndiye kuti iye adzadziwa mtendere, chimwemwe ndi kusungika. pokhapokha titachita naye Yesu mu chisoni chake ndi zowawa zake za mu Getsemane pomwepo tidzamva chimwemwe cha kuuka kwake.

Potsiriza penipeni, zotsatira zake za kulapa ndi kukhala woyamika kotheratu ndi kudzipereka kwa Khristu ndi ku chifuniro cha Mulungu. Pa ichi chiphatikizanso Mpingo monga kunaikidwa mu Chipangano Chatsopano. Pamene tinaikidwa kufa ndipo popanda njira yotulukiramo, Yesu anati: "ldzani kwa lne ndipo ndidzakupumulitsani inu" (Mateyu 11:28). "Timkonda ife chifukwa anayamba lye kutikonda" (1 Yohane 4:19).

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.