Masiku Awiri Mu Gehena

Pa nkhani zonse za kutsitsimuka kwa akufa zimene ndinamva, imene inandichititsa chidwi kwambiri ndi nkhani ya George Lenokisi. Iye  anali wakuba wodziwika amene anakhala ku boma la Jefferson County, ankakonda kuba abulu. Nthawi imeneyo anali mundende atamangidwa kachiwiri. Poyamba anamangidwa ku boma la Sedgwick County chifukwa cha mlandu womwewo, kuba abulu.

Nkhaniyi idachitika pakati pa chaka cha 1887 ndi 1888 inali nyengo yozizira, iye adali kugwira ntchito mumgodi wa malasha. Pa malo pamene iye adali kugwira ntchito padali poopsa kwa iye. Kotero adachita lipoti kwa mkulu wa ntchito, iye ataona malowo adam'uza kuti malowo ali bwino, ndipo ayenera kupitiriza kugwira ntchito yake. Iyeyu adamvera, koma sadapitirira kugwira ntchito nthawi yaitali, pamenepo denga la mgodi lidagwa lidamukwirira. Adakhala pomwepo nthawi yaitali.

    Pa nthawi ya chakudya cha madzulo adasowa. Atamufufuza anam'peza pansi pa zinyalala za denga la mgodi. Atamuchotsa dokotala wa m'ndendemo adam'yeza, nam'peza kuti munthuyo wafa kale. Thupi lake adalitengera kuchipatala komwe adalisambitsa bwino ndi kuliveka zovala, pokonzekera kukaliika ku manda. Adamukonzera bokosi loyembekezera kugonamo iye ndi kufika nalo kuchipatala. Abusa a kundende adafika  kudzachita mwambo wa maliro. Woyang'anira za m'ndende adauza akaidi ena kuti ayenera kunyamula mtembo uja ndi kuwuika m'bokosi. Iwowa adamvera, nanyamula mtembowo, ena ku miyendo ena kumutu, koma ali pafupi kuti afike pamene padali bokosi amene adanyamula kumutu adapunthwa mwangozi nagwetsa mtembowo. Mutu wa mtembowo udagunda pansi ndipo onse amene adali pamalopo adadabwa kwambiri pakumva wakufa uja akuzuma. Nthawi yomweyo maso ake adatseguka naonetsa kuti ali ndi moyo. Dokotala adaitanidwa kuti abwere. Zitatha mphindi makumi atatu (30 minutes) dokotala adafika, napeza kuti wakufayo adaitanitsa madzi akumwa ndipo adali pakati pa kumwa madziwo.

     Nthawi yomweyo bokosi lija lidachotsedwa ndipo lidagwiritsidwa ntchito poikamo mtembo wa mkaidi wina. Kenaka adamuchotsa zovala zake za kumanda zija ndipo adamupatsa zovala zake za kundende. Atamuyeza adapeza kuti mwendo wake umodzi udathyoka malo awiri, ndiponso anali ndi mikwingwirima ina. Adakhala kuchipatala miyezi isanu ndi umodzi. Atachira adatumizidwanso kukapitiriza ntchito yake ku ndende.

Nkhani yonse ya: Masiku Awiri Mu Gehena

     Wandende mnzake wa Lenokisi adandiuza chinthu cha chilendo chomwe chidam'chitikira pa nthawi yomwe adali ngati wakufa. Nkhaniyi idandichititsa chidwi moti ndidafunitsitsa kukomana naye  Lenokisi kuti ndimve nkhaniyi kuchokera pakamwa pake. Mwayi woti ndikomane naye sudapatsidwe kwa ine kwa miyezi ingapo, koma kenaka ndidakomana naye. Nditachotsedwa pantchito ya mu'mgodi ndidapatsidwa ntchito yolemba malipoti ena kuofesi ina yakundende. Tsiku lina nkhani yakuuka kwa akufa kwa munthu uja idakambidwa, nthawi yomweyo adadutsa pakhomo paofesi, ndipo adandilozera kwa iye. Posakhalitsa ndidam'patsa kalata yoti afike kumene ndidali kugwira ntchito. Atafika,  ndidali ndi nthawi yokambirana naye, ndipo kuchokera pakamwa pake ndidamva nkhani yake yodabwitsa. Adali wachinyamata wosapyolera zaka makumi atatu, koma anakhwima m'makhalidwe a umbava. Adali munthu wophunzira bwino komanso wanzeru.

     Mbali yodabwitsa ya nkhani yake idachitika panthawi imene adali wakufa. Popeza ndidali wotola nkhani mwachidule, ndidali kulemba zonse zomwe adali kundiuza.

     Iye adati: “ Kuyambira m'mawa wonse ndidali nditadziwa kuti kanthu kena koopsya kadzachitika. Chifukwa cha nkhawa imeneyi ndidapita kwa woyang'anira wamkulu wa mumgodi, Bambo Grason, kuti ndimulongosolere momwe ndidali kumvera. Ndidam'pempha kuti adzaone malo omwe ndidali kugwirapo ntchito yokumba malasha. Adabwera, nakhala ngati wapimadi malowo, nandilamula kuti ndiyenera kupitiriza kugwira ntchito. Adandiuza kuti palibe choopsa chili chonse, naganiza kuti mutu wanga wasokonekera. Ine ndidabwerera ku ntchito yanga, ndipo ndidali kukumba kwa ntahwi yochepa, pamenepo ndidaona mwadzidzi kunali mdima waukulu. Kenaka padaoneka ngati chitseko chachitsulo chachikulu chidatseguka, ndipo ndidalowa pa khomo lake. Pamenepo ndidadziwa m'moyo mwanga kuti ndidali wakufa ndipo ndidali m'dziko lachilendo. Sindidathe kuona munthu wina ali yense kapena kumva china chilichonse, ayi. Mphamvu ina yosadziwika kwa ine idandiyendetsa kuchoka pakhomopo ndipo ndidayenda patali kufika m'mphepete mwa mtsinje waukulu. Kudali ngati usiku pamene pali nyenyezi zambiri, sikudali kowala kweni-kweni kapena mdima. Sipadapite nthawi yaitali, ndili kutsidya la mtsinjewo, ndidamva phokoso lotakasidwa madzi popalasa bwato.  Posachedwa munthu amene adali m'bwatomo adapalasira kufika pafupi ndi pomwe ndidaima.

     “ Nthawi imeneyo ndidali wopanda mawu. Iye adandiyang'ana kamphindi kochepa, nati kwa ine, 'ndabwera kudzakutenga,' nandiuza kuti tikwere bwatolo kuti tiolokere tsidya lina. Ndidamumvera. Padalibe mawu ena amene adalankhulidwa. Ndidali kufuna kuti ndimufunse dzina lake ndiponso kumene ndili, koma sindidathe chifukwa lilime langa lidamamatira m'kamwa mwanga, kotero kuti sindidathe kunena liwu lililonse. Kenaka tidafika tsidya lina la mtsinjewo ndipo ndidachoka m'bwatomo. Nditaturukamo wopalasa bwato uja anandikanganukira kumaso kwanga, nandichokera.   

 “Atandisiya choncho, ndidasowa chochita. Poyang’ana patsogolo panga, ndidaona njira ziwiri zidaloza ku chigwa cha mdima. Njira imodzi idali yotambalala imene imaoneka kuti ndi yotakata. Njira ina idali yopapatiza yopita mbali ina, koma ine ndidatsata njira yaikulu yotakata ija. Sindidapite patali pamene ndidaona kuchuluka kwa mdima udali nkukulabe. Komabe ndidali kuona kuwala kochokera patali, potero ndidaunikiridwa pa ulendo wangawo.

“Posachedwa ndidakomana ndi chinthu china, maonekedwe ake sindingathe kulongosola, koma ndingalongosole pang’ono maonekedwe ake oopsya. Maonekedwe ake adali ngati munthu, koma adali wamkulu koposa munthu aliyense amene ndidamuonapo. Utali wake udali monga ngati mamita atatu. Adali ndi mapiko akulu kumbuyo kwake. Adali wakuda monga ngati malasha omwe ndinali kukumba. Adali wamaliseche wosavala chirichonse. M’dzanja lake adagwira nthungo yotalika pafupifupi mamita asanu. Maso ake adawala ngati mipira ya moto. Mano ake adali oyera kwambiri ndipo utali wake monga ngati inchi imodzi. Mphuno yake idali yaikulu ndithu yotambalala yokhala yophwaphwatika. Tsitsi lake lidali lokhakhala, losaoneka bwino, lalitali, ndipo linagwera m’mapewa ake akulu. Mawu ake anabangula monga mau a mkango.

“Idali nthawi yowala mu mdimamo imene ndidamuona poyamba. Ine ndidanjenjemera kwambiri monga tsamba la mtengo logwedezeka ndi mphepo. Adakweza nthungo m’dzanja lake kuloza kwa ine nakhala ngati afuna kundiponyera. Mwadzidzidzi ndidaima. Ndili wonjenjemera chomwecho, adanena ndi mawu woopsya amene ndikuwakumbukirabe, nandiuza kuti ndimutsate iye chifukwa watumidwa kuti anditsogolere pa ulendo wangawo. Ndipo ndidamutsata. Ndi chiyani chomwe ndikadachita? Titayenda patali pang’ono, phiri lalikulu lidaonekera patsogolo pathu. Lidaoneka phiri longa logawidwa pakati, ndipo pa mbali ina ya phirilo inali khoma lalitali. Pakhomapo padali mau olembedwa: ’MALO A GEHENA’. Wonditsogolera adafika pakhoma la phirilo nagogoda katatu ndi chogwirira cha nthungo yake. Ndipo chitseko chachikulu chidatseguka cham’tsogolo, ndipo tidalowa mkati. Pamenepo adanditsogolera kupyolera mkati mwa phirilo.

“Pa kanthawi tidayenda mumdima waukulu. Ndidali kumva mgugu wa mapazi oyenda kotero kuti ndidatha kutsatira wonditsogolerayo. M’njira yonseyo ndinali kumva kubuula monga ngati wina alinkufa. Popitirira ndi ulendo wathu kuliraku kudali kuchuluka, ndipo onsewo adali kulira poitanitsa, ‘Madzi, madzi, madzi.’ Tsopano titafika pakhomo lina, popitirira, ndidamva mau wolira mochuluka ngati anthu okwana zikwi chikwi patali. Ndipo kulirako kudalinso kupempha, ‘Madzi, madzi, madzi.’ Posachedwa khomo lina lalikulu lidatseguka wonditsogolera atagogoda. Ndidapeza kuti tidayenda mopyola mkati mwa phiri lija, ndipo ndidaona chigwa chachikulu chili patsogolo panga.

“Pamalo amenewa wonditsogolerayo adandisiya ndekha, napita kukatsogoleranso mizimu ya anthu ena otayika kunjira yomwe tidadzerayo. Ndidakhala pa chigwa chotsegukacho kanthawi pamene munthu wina wokhala ngati woyamba uja adabwera kwa ine; koma m’malo mokhala ndi nthungo, iye adabwera ndi lupanga lalikulu. Iye adabwera kudzandiuza za chionongeko changa cham’tsogolo. Adalankhula ndi mau oopsya amene adakhudza moyo wanga. Adati, ‘Iwe, uli ku Gehena. Chiyembekezo chako chonse chathawa. Pobwera kuno udayenda kupyola m’phirimo, ndipo udali kumva kulira kwa anthu otayikawo, amene adali kupempha madzi kuti athe kuziziritsa malilime awo otenthedwa. Panjira imeneyo pali khomo lolowera kupita ku nyanja ya moto. Posachedwa kumeneko kudzakhala chionongeko chako. Musanaperekezedwe ku malo amazunzo awo, kumene simudzatulukanso (chifukwa kulibenso chiyembekezo kwa amene alowamo) mudzaloledwa kuima malo achigwa ngati ano, kumene kwapatsidwa kwa onse otaika, kuonetsedwa zabwino zomwe akanazilandira, koma m’malo mwake alinkulandira chilango.

 “Zitatha izi ndidapezeka ndiri ndekha. Kapena chifukwa cha kuopsedwa kwambiri pa njira, sindikudziwa, koma tsopano ndidapezeka wolefuka. Kufooka ndi kusamva kudagwira thupi langa, mphamvu zanga zidachoka, ziwalo zanga zidalephera kulimbitsa thupi langa. Ndidathedwa, ndipo ndidagwa pansi. Ndidakhala ngati ndakomoka, monga munthu wogona koma ali ndi moyo, ndipo ndidaona ngati ndikulota.  Poyang’ana kumwamba patali ndi ine, ndidapenya mzinda wokongola ndithu womwe timauwerenga m’Buku Lopatulika. Makoma ake adanyezimira ngati miyala ya yaspi ndipo pambali pa mzindawo ndidaona malo akulu okutidwa ndi maluwa okongola kwambiri. Ndidaonanso mtsinje wa moyo ndi nyanja yowala ngati galasi. Ndipo angelo ochuluka adali kulowa ndi kutuluka pa zipata za mzindawo, ali kuimba nyimbo zokoma. Pakati pawo ndidaona mayi wanga wokondedwa amene adafa zaka zapitazo ndi mtima wawo wosweka chifukwa cha zoipa zomwe ndidali kuchita. Mayi adandiyang’ana nandikodola kuti ndipite komwe kudali iwo. Koma ine sindidathe kusuntha pomwe ndidali. Kudaoneka ngati ndili ndi chinthu cholemera kwambiri chomwe chidandikanikiza pansi. Pamenepo mphepo yabwino idawomba kuloza kwa ine ndi kununkhira kochokera m’maluwa okongola aja kudandifikira ine. Ndidamva kuyimba kokoma kwa angelo, ndipo ine ndidalira ndi kunena, ‘Ndikadakhala m’modzi wa iwo.’

 “Ndidakali kumwera chikho chokomachi poona zokoma zonse, mwadzidzidzi chidachotsedwa kukamwa kwanga. Munthu uja anandidzutsa kutulo tanga, ndipo nandichotsa ku dziko labwino lomwe ndidali kuona masomphenya. Anandiuza kuti, ‘Ndi nthawi tsopano yokalowa komwe iwe udzakhala. Munditsate ine.’ Pamene ndidayamba kuyenda, ndidalowanso munjira ya mdima. Ndidamtsatira wonditsogolera kanthawi, pamene tinafika pakhomo lotseguka pambali. Popitirira pamenepo tidapezeka tili kulowa pakhomo pena, ndipo taonani ndidaona nyanja ya moto! Nditapenya polekezera maso anga ndidaonadi nyanja ya moto ndi miyala ya moto. Mafunde akulu a moto adali kukweranakwerana, funde lina pa linzake. Malawi a moto adali kukwera m’mwamba monga mafunde a m’nyanja owinduka ndi mphepo yaikulu. Ndidapenya anthu alikulimbana ndi mafunde a motowo, koma mafundewo adali kuwakanikiza pansi pakuya munyanja ya moto. Pamwamba pa mafunde akulu a moto padaoneka anthu, kwa kanthawi adali kutukwana moipitsitsa Mulungu wolungamayo. Kulira kwao kolilira madzi kudali komvetsa chisoni. M’nyanja yamoto imeneyi mudali kumveka mau olira ndi kulira kosalekeza kuchokera ku mizimu yotaikayo. 

  “Pamenepo ndidatembenuza maso anga kuyang’ana pakhomo pamene ndidalowapo posachedwa, ndipo ndidawerenga mau olembedwa motere: ‘MALO ANO NDI A CHILANGO CHAKO, KUNTHAWI YOSATHA.’ Posakhalitsa ndidaona nthaka ilikuchoka ku mapazi anga, pomwepo ndidapezeka ndili kumira munyanja yamoto. Ludzu losaneneka lofuna madzi lidabwera kwa ine. Ndili kuitanitsa madzi, maso anga adatseguka, ndipo ndidapeza kuti ndili ku chipatala cha kundende.

   “Sindidauze aliyense nkhani imeneyi kale lonse, chifukwa ndidali kuchita mantha kuti akulu oyang’anira m’ndende akadandiganizira kuti ndazungulira mutu, ndi kundisekera m’chipatala cha amisala. Ine ndidapyola mu zonsezi, ndipo ndili wokhutitsidwa kuti Kumwamba kulipo, Gehena ilipo, ndi Gehena yakaleyo imene Buku Lopatulika limanena nthawi zonse. Koma choonadi ndi ichi, ine sindidzapitanso ku malo a Gehenawo ayi.

    “Pamene ndidatsegula maso anga mu chipatala ndi kuona kuti ndili ndi moyonso mdziko lino, nthawi yomweyo ndidapereka mtima wanga kwa Mulungu, ndipo ndidzakhalabe Mkhristu mpaka imfa. Sindidzaiwala konse kuopsa kwa Gehena ndi zokoma zakumwamba zomwe ndidaziona. Ine ndakonzeka kukakomana ndi wokondedwa mayi anga omwe ali kale komweko. Ndipo ndidzaloledwa kukhala pansi pa m’mbali mwa mtsinje wokongolawo, ndipo ndidzatha kuyenda ndi angelowo kuwoloka chigwacho ndi kupyola mapiri omwe akutidwa ndi kununkhira kwa maluwa omwe kukongola kwake kosayerekeza ndi kanthu kalikonse ka m’dziko lino lapansi. Ndidzakhala ndikumvera nyimbo za anthu owomboledwa. Panopa ndasiya zokondweretsa za dziko zomwe ndidayendamo kale ndisadabwere ku ndende, chifukwa zokoma za Kumwamba zidzaposa zonsezo. Ndawasiyanso abwenzi omwe ndidali kuchita nawo zoipa, ndiyenera kugwirizana ndi anthu a makhalidwe abwino ndikadzatuluka mundende.”

    Tikupereka nkhani imeneyi kwa awerengi onse monga momwe ife tidailandira ndi kuimva kuchokera kwa Bambo Lenokisi mwini wake. Mulungu wamphamvu yonse adalitse uthenga umenewu kuti uthe kutsitsimutsa mizimu ya anthu otaika kuti apeze chipulumutso.

  Ha! Kodi anthu angakayike bwanji kuti kuli Gehena? Tili ndi Buku Lopatulika ndilo mau a Mulungu ndiponso mabvumbulutso monga a Bambo Lenokisi amene aphunzitsa za Gehena. Abambo ndi amai, khalani chete! Choonadi chilipo! Moyo wanu udzawerengedwa! Mulungu akufuna kukupulumutsani, ndipo adzaku-khululukirani ngati muvomereza kuti ndinu wochimwa. Njira yokhayo yoloza kuchipulumutso ndi kutsukidwa kuchokera ku machimo pakuvomereza mwazi wa Yesu Kristu monga nsembe ku machimo anu. Mukalandira chikhululukirochi kuchokera kwa Mulungu, Adzakupatsani mtendere ndi mpumulo m’mtima mwanu. Mungakhale womasuka m’moyo uno, komanso wokonzeka kulandira chisangalalo cha kumwamba m’malo mwa ku khala ku Gehena osati masiku awiri okha koma m’paka muyaya.

Fanizo la mwini Cuma ndi Lazaro waumphawi

Luka 16:19-31

Ndipo panali munthu mwini cuma amabvala cibakuwa ndi nsaru yabafuta, nasekera, nadyerera masiku onse; ndipo wopempha-pempha wina, dzina lake Lazaro, adaikidwa pakhomo  pace wodzala ndi zironda, ndipo anafuna kukhuta ndi zakugwa pa gome la mwini cumayo; komatu agarunso anadza nanyambita zironda zace. Ndipo kunali kuti wopemphayo adafa, ndi kuti adatnegedwa iye ndi angelo kunka ku cifuwa ca Abrahamu; ndipo mwini cumayo adfanso, naikidwa m’manda.

   “Ndipo m’Hade anakweza maso ace, pokhala nao mazunzo, naona Abrahamu patali, ndi Lazaro m’cifuwa mwace. Ndipo anakweza mau nati, Atate Abrahamu, mundicitire cifundo, mutume Lazaro, kuti abviike nsonga ya cala cace m’madzi, naziziritse lilime langa; pakuti ndizunzidwadi m’lawi ili la moto. Koma Abrahamu anati, Mwana, kumbukila kuti unalandira zokoma zako pakukhala m’moyo iwe, momwemonso Lazaro zoipa; ndipo tsopano iye asangalatsidwa pano, koma iwe uzunzidwadi. Ndipo pamwamba pa izi, pakati pa ife ndi inu pakhazikika phompho lalikuru, kotero kuti iwo akufuna kuoloka kucokera kuno kunka kwa inu sangathe, kapena kucokera kwanuko kuyambuka kudza kwa ife, sangathenso. Koma anati, Pamenepo ndiku-pemphani, Atate, kuti mumtume ku nyumba ya atate wanga; pakuti ndiri nao abale asanu; awacitire umboni iwo kuti iwonso angadze ku malo ano a mazunzo. Koma Abrahamu anati, Ali ndi Mose ndi aneneri; amvere iwo. Koma anati, Iai, Atate Abrahamu, komatu ngati wina akapita kwa iwo wocokera kwa akufa adzasandulika mtima. Koma anati kwa iye, Ngati samvera Mose ndi aneneri, sadzakopeka mtima ngakhale wina akauka kwa akufa.

Malemba ena: Cibvumbulutso 21:7-8, Cibvumbulutso 20:10,12,13; 2 Petro 3:10-12.

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.

Kulapa: Khomo la Chifundo

Wokondedwa Moyo'we: Kodi ukudziwa kuti wapezeka wochimwa ndi Mulungu Woyerayo, ndi kuti kwaikidwa kwa iwe kufa? Ngati munthu wochimwa afuna kuithawa imfa ya muyayayi ndi kupulumutsidwa ku nthawi zosatha, iye ayenera kulandira chifundo cha Mulungu'chi. Chifundo chimatiteteza ife pa chirmene tikadalandira. Komatu Mulungu samangoika chifundo chake pa anthu popanda choyenereza ayi, ngakhale kuti chipulumutso nchaulere, chopanda mtengo wake (chosagula) ndiponso chosati nkuchigwirira ntchito. Chotiyenereza chakuti Mulungu atipatse ife chifundo chake chipezeka mu liu limodzi lokha: Lapani.

Yohane Mbatizi anadza nalalikira Mau a Mulungu ndipo uthenga wake unali wokhweka, koma wamphamvu. "Lapani inu chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira" (Mateyu 3:2). Yesu, Mwana wa Mulungu, anayamba utumiki wake ndi uthenga womwewo, "Lapani pakuti ufumu wakumwamba wayandikira" (Mateyu 4:17). Kulapa ndicho chotiyenereza cha chipulumutso monga Mtumwi petro ananena, "Chifukwa chake lapani, bwererani kuti afafanizidwe machimoanu" (Machitidwe 3:19). Kulapa ndi khomo loyenera kutsegulidwa ngati chifundo chingaonjezedwe ndi chipulumutso kupatsidwa.

Mdziko lapansi lathuli muli unyinji wa anthu, bwenzi langawe, mnjira zambiri timasiyana wina ndi mnzake. Komabe pali mbali ina imene tonse pamodzi timagawana popanda wotsala. Mau a Mulungu amationetsera ife bwino mbali imeneyi pamene amati: "Pakuti ONSE anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu" (Aroma 3:23). Ndipo tamveraninso, "Palibe M'MODZI wolungama, inde palibe m'modzi" (Aroma 3:10). Mulungu ananena kupyolera mwa mneneri wake Yesaya ndi kuti, "Tonse tasochera ngati nkhosa, tonse tayenda yense mnjira ya mwini yekha" (Yesaya 53:6). Kodi ulikudziwa cholinga chenicheni cha malemba oyerawa? "ONSE anataika". "PALIBE wolungama". "ONSE anachimwa". Wokondedwa wowerenganu, kodi ichi sichili kukukhudzani? Mzimu wanu, mayo wanu ndi za Mulungu. Mwamuna kapena mkazi ngakhale mwana kapena wamkulu amene sazindikira Mulungu monga mwini wa moyo wake aneneyo ali mkusamvera ndi mtchimo. "Moyo wochimwawo ndiwo udzafa" (Ezekieli 18:4).

Machimo anu akulekanitsani inu ndi Mulungu. Mumamva kufunafuna mkati mwanu kotero kuti simungathe kukufotokoza ayi. Mungathe kuona ngati ndinu wotayika ndi kuti Mulungu sakumva. Chifukwa chake Mulungu achitchula, "Taonani mkono wa Yehova sufupika, kuti sungathe kupulumutsa; khutu lake silili logontha, kuti silingamve; koma zoipa zanu zakulekanitsani inu ndi Mulungu wanu; ndipo machimo anu abisa nkhope yake kwa inu kuti lye sakumva" (Yesaya 59:1-2). Ndiponso, "Mphotho yake ya uchimo ndi imfa" (Aroma 6:23). Pamene muli kulingilira za moyo wanu ndi machimo anu, lingiliraninso za Mulungu. Mulungu alibe tchimo, choncho lye ndi Woyera, wolungama ndi wolunjika. Mulungu amati tchimo liyenera kuweruzidwa. "Pakuti Mulungu adzaweruza mlandu wa zochita zonse, ndi zobisika zonse, kaya zabwino ngakhale zoipa" (Mlaliki 12:14). Pali phompho lalikulu loikika pakati pa inu ndi Mulungu, ndi imfa yamuyaya, pokhapokha titapeza njira yomwe ipyola phompholo ndi kukoka wochimwayo pa maso pa Mulungu Woyerayo (Luka 16:26). lnde ilipo njira, chilipo chiyembekezo chanu!

Nkhani yonse ya: Kulapa: Khomo la Chifundo

Pamene tiona kuti Mulungu anaika chiweruzo cha imfa chifukwa cha tchimo, lyenso ndi Mulungu wachikondi. "Mulungu ndiye chikondi" (1 Yohane 4:16). Mulungu akukondani, mnzanga, ngakhale mukukhala mu uchimo. Chikondi chake chidakukonzerani njira yoti mupulumutsidwe nayo (Yohane 3:16). Mulungu, wosanamayo, adzaika chiweruzo chake pa tchimo, ndipo ngati chilungamo chake sichidzakhala pa munthu, pomwepo iye adzafa. Chomwecho Mulungu safuna wina aliyense kuti ataike, anatuma Mwana wake Yesu kutitengera thonzo la uchimo kuti tikhale ndi moyo. Malemba akuti, "Chifukwa chake onani chifatso chake ndi kuuma mtima kwake kwa Mulungu" (Aroma 11:22). Ubwino wa Mulungu ndi wakuti apulumutse munthu koma chiweruzo chake chinkafuna chilango.

Yesu anadza ku dziko lapansi ndi cholinga chakuombola miyoyo yathu. Iye ndi Woyera ndi wopanda tchimo, Mwana-wa-Nkhosa wa Mulungu wopanda chilema. Chikondi cha Mulungu chapa ife chinaoanekera pamene lye anatenga machimo athu ndi kulakwa kwathu ndi mphotho yake ya imfa ndi kuziika izi pa Yesu. Taonani ubwino wake! Ndipo monga Yesu anamvera chifuniro cha Atate wake, lye analandira mphotho ya machimo athu. Yesu anakhala wochimwa m'malo mwathu ndi kukwaniritsa chiweruzo cha Mulungu. Iye anapachikidwa pa mtanda pa maora asanu ndi limodzi (6 hours) namva kuwawa ndi ululu kufikira mphotho yake ya machimo athu itaperekedwa, ndipo pamenepo Yesu anafa. Taonani kuuma mtima kwake kwa Mulungu!

Wokondedwa wowerenganu, kodi mukuona kuti Yesu anakuferani inu, ndi kuti lye anafa CHIFUKWA cha machimo anu? Kodi makamaka yemwe adapachika Yesu ndani? Kodi amene anakhudzidwa ndi akuluakulu a Ayuda, kapena Pilato kapena asilikari a Aroma okha? Petro mtumwi tsiku lina analalikira kwa chikhamu cha anthu zikwizikwi. Uthenga wake wa Petro unali woona: "lye (Yesu), anaperekedwa ndi chikhamu komanso ndi nzeru ya kudziwiratu ya Mulungi, INU munamtenga ndi manja anu oipawo munampachika ndi kumupha" (Machitidwe 2:23). Wokondedwa moyowe, yang'anani kwa Yesu yemwe anapachikidwa ndipo bvomerezani kulakwa kwanu ndi kuchita naye mu imfa yake!

Kulapa koonadi kumayambira makamaka pa mfundo imeneyi, pamene musunga mu mtima mwanu za malo owopsyawo ndi zomwe zinachitikazo. Ndi mphamvu ya Mzimu wa Mulungu mudzazindikira kuti mukanayenera kufa munali inu osati Yesu ayi. Koma Yesu anatenga malo anu! Ngati inu muzindikira ichi mumtima mwanu, kudzakubweretserani chisoni ndi kuti tchimo simudzalifunanso ayi. Pakulingirira kuti wina adakonzera wina imfa ndi chinthudi chochititsa mantha, makamaka kuti lye anali Mwana weniweni wa Mulungu. Miyoyo yomwe imagwira masomphenya awa imalapa ndi kubvomereza machimo awo. Ndi monga momwe tilingirira za chiweruzo cha Mulungu chokhuthulidwa pa Yesu ndipo pakuchidziwa ichi tidayenera kulira ndi ife omwe tidayenera imfa, "Mulungu mundichitire chifundo ine wochimwa" (Luka 18:13). lzi ndi ntchito zoyamba za kulapa. Ngati kulapaku kupitirira, kumakwaniritsa pa kusiyiratu njira zathu zoyamba za uchimozo, ndi kutembenukira ku njira za Mulungu. Munthu yemwe watsukidwa ndi kuyeretsedwa kuchokera ku njira zake zoipazo, iye adzazifulatira izo ndi kutembenukira ku zinthu zakumwamba. ichi mwachidule ndi njira yolapa yomwe imachitika ndi Mulungu mu mitima ya onse akudza kwa lye. Pokhapokha munthu atalapadi, ndiye kuti iye adzadziwa mtendere, chimwemwe ndi kusungika. pokhapokha titachita naye Yesu mu chisoni chake ndi zowawa zake za mu Getsemane pomwepo tidzamva chimwemwe cha kuuka kwake.

Potsiriza penipeni, zotsatira zake za kulapa ndi kukhala woyamika kotheratu ndi kudzipereka kwa Khristu ndi ku chifuniro cha Mulungu. Pa ichi chiphatikizanso Mpingo monga kunaikidwa mu Chipangano Chatsopano. Pamene tinaikidwa kufa ndipo popanda njira yotulukiramo, Yesu anati: "ldzani kwa lne ndipo ndidzakupumulitsani inu" (Mateyu 11:28). "Timkonda ife chifukwa anayamba lye kutikonda" (1 Yohane 4:19).

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.

Bwanji Za Mankhwala, Zoledzeretsa, Ndi Chiwerewere?

"Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa..." (Aroma 6:23)

Tiyeni tinene zoonadi. Zirombo zoopsya kumwa zoledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere ziri  nkuopsyeza ndiponso kuononga chimene Mulungu anachilenga kukhala chokoma ndiponso chabwino. Monga mchitidwe wa Octopus wamphamvuyo, izi zimakoka ang'ono komanso aakulu ndi kuwafumbatira.

Anthu ambiri amakakamizidwa pambali iliyonse ndi zokhumba zao, monga manyuzi pepala komanso ndi kuitanira kwa television. Maso ndi makutu zimalunjika kumene kuli zosokoneza zokhazokha zomwe zotsatira zake ndi kukhala ndi moyo wa uzimu komanso wa kuthupi wobwerera m'mbuyo. Temberero la chakumwa choledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere zaleka chitsanzo chokoma cha m’midzi yathu popanda kuongoledwa ndipo ziri nkupita ku chionongeko.

Kodi nanga ndi mbadwo wokha wa ana womwe utsutsidwe? Ayi. Naonso makolo ambiri asiyanso chikhalidwe chokoma, natsata chikhalidwe choipa, machismo ambiri ochitidwa ndi ana ambiri lero, makolo awo amangowalekerera osadziwa kuti alikupanga ana awo kuti adzakhale zidakwa, ogwiritsa ntchito mankhwala osaloledwa, ndi osuta pakulephera iwo kudzudzula pa kumwa zoledzeletsa ndi kusuta.

Mwadala, pakufuna kukhala osamvera malamulo olunjika a Mulungu makolo naonso ali pa njira yotsetsereka yopita ku mnyozo panopa komanso moyo ulinkudzawo. Kulira kopfuula kuyenera kukwera kumwamba. Tingadzipulumutse bwanji ife ndi ana athu?

M'manyumba mwathu, m'masukulu ndiponso m’makoleji sangathe kutulutsa chitsanzo chabwino choyenera nzika za dziko monga momwe maiko athu afunira ngati kumwa zoledzeretsa ndi kugwiritsa ntchito mankhwala zirigoyang'anidwa ndi kulimbikitsidwa ndi makolo opanda chikhalidwe chabwino, aphunzitsi ndi iwo anzeru zakuya . (Professors}, kuonongeka kwachikhalidwe chabwino m'masukulu kuli nkuopsezanso. Sipanathe zaka zambiri pamene aphunzitsi ndi anzeru zakuya akadachotsedwa ntchito chifukwa cholekerera ana asukulu kukhala ndi makhalidwe oipa.

Mliri umene watenga malo kwambiri mbadwo wathu uno ndi kumwa mwa uchidakwa kumenenso kumaononga chikhalidwe chabwino. Kuononga chikhalidwe ndi kumwaza ndalama pamene miyanda miyanda ya anthu alikusowa chakudya. Ichi ncha umphawi komanso chopereka magawano m'manyumba mwathu, ndiponso lonyoza dalitso loyera la Mulungu pa mtundu wa anthu.

Nkhani yonse ya: Bwanji Za Mankhwala, Zoledzeretsa, Ndi Chiwerewere?

Kuphatikiza kuipa kwa kumwa zoledzeretsa kwaonjezeranso kagwiritsidwe ka mankhwala osaloledwa. Kuipa kwa mankhwalawa kumaposa phindu lomwe mankhalawa amapereka. Kugwiritsa ntchito mankhwala osaloledwawa kungapangitsenso kuweruza molakwika ndiponso kuonongeka kwa nzeru. Ogwiritsa ntchito mankhwalawa naonso amabvomereza kuti ndi ulendo waku imfa mu nzeru, kuthupi lanyama, mu mzimu komanso kungathe kuononga ubongo. Kuphana ndi kudzipha ndizo zotsatira zake zoopsya za mchitidwe umenewu.

Khristu, m"Chipangano Chatsopano, anaika chitsanzo cha makhalidwe abwino. Naikanso ndime ya chikhalidwe chabwino. Mulungu analenga munthu kuti mtundu wa anthu uchuluke ndi kuti anthu adzikwatirana mwamuna ndi mkazi. lye anaikanso kuti padzikhala kufunana koyenera pa moyo Wa m’banja. Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; koma adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu. Aheb. 13:4

Anthu ambiri ali kuzunzika ndi miZimu ya chilakolako. Zotsatira zake zimakhala nkhondo yeniyeni pakati pa thupi ndi Mzimu. Thupi limafuna kukhala ndi ufulu wa kuchita zokondweretsa zake popanda choletsa, pamene Mzimu amadziwa bwino kuti malamulo onse a Mulungu ayenera kutsatidwa bwino. Chiwerewere sichingathe kuthetsa kutentha mtima kwa chilakolako, monganso mowa wa whisky umalephera kuchotsa ludzu la mowa. Apa choonadi ndiye chili pa mbali ina osati iyi ayi.

Chiwerewere, chigololo, dama la amunaokhaokha ndi chiwerewere china chirichonse pakati pa munthu ndi nyama ndi choletsedwa m'Mawu a Mulungu. Chiwerewere chimabweretsa kuwawa, kupweteka mtima, umphawi, kuchimwa, ndiponso kutenga matenda. Lev 18:23, Agalatiya 5.19-21. Chiyero chimabweretsa chisoni kuti anthu oyenera ndi olongosoka ali kukhala mu umphawi pamene munthu wopanda pache ali nazo zonse zomuyenereza. Mtumwi Paulo m'buku la Aroma akunena za momwe Mulungu adzaweruzire ochita chiwerewere cha amuna okhaokha. Chifukwa cha ichi, Mulungu nawapereka iwo ku zilakolako za manyazi: Pakuti ngakhale akazi awo anasandutsa machi- tidwe awo achibadwidwe kukhala osalingana ndi chibadwidwe: Chimodzimodzinso amuna, anasiya chikhalidwe cha chibadwidwe cha akazi, natenthetsana wina ndi mzake, amuna okhaokha ndi kuchita cbosayenera kuti akalandire mphoto yoywera m'chitidwe umenewu. Monga momwe iwo sanafuna kukhala naye Mulungu m'nzeru zao .. Mulungu anawapereka ku mtima wokanika, kuchita zosayenera: Pakudziwa chiweruzo cha Mulungu, kuti ochita zimenezi ayenera kufa, chifukwa samangodzichita kokha ayi, komanso amakondwera nazo. (Aroma 1:26,28,32). Ili linali tchimo lonyansa kwambiri la Sodomu ndi Gomora limene linabweretsa kulanga kwa Mulungu pakati pawo (Gen. 19). Monga mwa Malemba Oyera kuti nkovuta kuti Mzimu Woyera kubwereranso m 'mitima yathu ndi kukhal m'moyo wa Chikristu ngati tiri kukhala natichitabe machimo amenewa.

Mkati mwa chiwerewerechi ndi khungu la uzimu, la tchimo lomwe kuli kusowa manyazi pakusapembedza Mulungu, tiyenera kutembenukira ku Buku Lopatulika lomwe liri ndi udindo wonse wosakaikitsa wa muyaya pa chabwino kapena choipa.

Wokondedwa wowerengawe, kukhala ndi moyo wokondwa, ndi inuyo kukhala ndi mtendere ndi Mulungu, muyenera kudza m'chiyanjano pamodzi ndi lye.

Chigonjetso chiri kukuyembekezani! Muyenera kuzindikira ndi kulapa kuti muli ochimwa ndipo mukhulupilire kuti Yesu anafa pa mtanda atasenza tchimo lanu. Pamene mutsegula mtima wanu kwa Mulungu ndi kulapa machimo anu, lye adzakukhululukarani. Ngati tibvomereza machimo athu, lye ali wokhulupirika ndi wolungama kutikhululukira ife machismo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chirichonse.

Muyenera kupereka mtima wanu wonse kwa Yesu, Mpulumutsi wanu, ndipo tsatirani bwino pomvera Mau Ake ndi Mzimu Woyera. Madalitso a moyo wosinthika ndi maganizo oyera omwe amabweretsa kusinthika kotheratu m'zochita zanu. Khristu adzakulimbitsani mtima pokomana ndi mabvuto a moyo ndi mphamvu yogonjetsa mayesero omwe angakuzungu- lireni. ldzani kwa Yesu tsopano pamene mumva kuitana kwake. "Funani Yehova popezekalye, itanani lye pamene ali pafupi. ... "  (Yesaya 55:6).

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.