Kodi Ndinu Okhulupirika Bwanji?

Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi  m'malo a m'katimo; ( Masalmo 51:6)

Kukhulupirika kumasonyeza kukhala pa choonadi mogwirizana ndi zochita-chita zonse za pa moyo. Kukhulupirika kumachokera mu mtima ndipo ndi chilamulo chokhazikika m'uthenga wa Yesu Kristu. Mulungu amadziwa maganizo ndi zolingirira za mu mtima. Amayang`anira kukhulupirika ngati chilamulo chofunika chifukwa Iye ndi Mulungu wokhulupirika (Deuteronomo 32:4). Iye adzadalitsa kukhulupirika kwathunthu kwa mu mtima wathu.

 

Kodi mumalankhula choonadi pamene mwapezeka kusiyana ndi pamene wina sanadziwe?

Kodi mumaonetsa khalidwe lonyenga m'malo mowonetsa moyo wanu weni-weni?

Kodi mumagula zinthu pa ngongole pamene mukudziwa kuti simungathe kulipira?  

Nkhani yonse ya: Kodi Ndinu Okhulupirika Bwanji?

Kodi mumachita mokhulupirika zonse zomwe mukudziwa kuti Mulungu akufuna kuti mumchitire?

Kodi muli okhulupirika molingana ndi chiphunzitso cha Buku Lopatulika?

Kodi inu ndi munthu amene mumadzi-onetsa kukhala ngati wokhulupirika?

Pali nkhani ina yogwira mtima imene ikupezeka m'chipangano chatsopano ya munthu dzina lake Hanania ndi mkazi wake Safira (Machitidwe 5:1-11). Anagulitsa munda wawo monga anachitira ena, nadzionetsa ngati anapereka ndalama zonse kumpingo, pamene iwo anagwirizana mwanseri kusunga zina. Hanania ndi Safira anabweretsa ndalama kwa akulu a mpingo, iwo ananena kuti anagulitsa pa mtengo womwe anapereka. Kusakhulupirika kwawo kunaweruzidwa nthawi yomweyo ndi chilango cha imfa. Pa nkhaniyi ya mpingo woyambirira, chipha-maso (kusakhulupirika) kunaperekedwa chilango cholimba. Mulungu amayang`ana mosalekerera pa zonama zotero. Ifenso monga Hanania ndi Safira tingachite chinyengo ngakhale sitinalankhule bodza. Timayiwala kuti tidzawerengedwa mlandu pa maso pa Mulungu. Mulungu amadziwa mitima yathu ndipo amayembekeza kukhulupirika kwathunthu.

Munthu wa chiphamaso amadzionetsera ngati wabwino pamene sali choncho. Iye amanena kuti ali pa choonadi, pamene amachita zokhotetsa choonadi kuti asapeze mavuto. Iye amalankhula zosowa za anthu ovutika, koma mavuto adzidzidzi akapezeka sapereka nthawi kapena ndalama. Wina amawoneka ngati akukhudzidwa kweni-kweni ndi achibale ake, pamene akuwanena miseche. Wina amawoneka ngati munthu wokhulupirika, koma akhoza kutenga ndalama za munthu wina akapeza mpata. Iye amakhala akuyesetsa kudzilungamitsa mwa iye yekha kuti ali ndi moyo wa pamwamba pa makhalidwe koposa ena, pamene akuchita mwa chinyengo. Munthu amene angakhale ndi makhalidwe amenewa ndi  wachipha-maso ndi wosakhulupirika.

Nthawi zonse chiphamaso cha munthu chimamvetsa chisoni Mulungu. Yesu anati, “ Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao; Koma mtima wao uli kutari ndi Ine” (Mateyu 15:8). Milomo ndi mtima wa munthu ndi kovuta zivomerezana. Kukhulupirika kuchokera m'kati mwa mtima ndi mafungulo opezera chisomo ndi kukomera mtima kwa Ambuye.

Mkristu wowona ndi chitsanzo cha kukhulupirika. Iye amapindula pa za uzimu molingana ndi kukhulupirika kwake pa maso pa Mulungu. Kufunika kwa kukhulupirika pamene tikudziwonetsera kwa  anzathu kuyenera kuchitika mo-samalitsa. M'mawu ndi ntchito zomwe timagwira tiyenera kulolera kudzipereka kwanthuthu kuti tikhale pa choonadi.

Pali phunziro limene tingathe kuphunzira kuchokera pa umboni pamene mphunzitsi anafunsa mnyamata wina, “Kodi ungathe kunena bodza chifukwa cha 5 Kwacha?”

“Ayi mayi,” anayankha mnyamata wamng`ono.

“Kodi ungathe kunena bodza chifukwa cha 15 Kwacha?”

“Ayi mayi,” anayankha mnyamata.

“Kodi ungathe kunena bodza chifukwa cha 150 Kwacha?”

“Ayi mayi,” ndilo linali yankho.

“Kodi ungathe kunena bodza chifukwa cha 150,000 Kwacha?.

“Inde,” ananena yekha mumtima, “Kodi ndingachite nayo chiyani 150,000 Kwacha?”

Pamene  uyu  anali  kusinkha-sinkha,  mnyamata wina wamng`ono amene anali kumbuyo kwake ananena, “Ayi mayi”.

“Ayi, chifukwa chiyani?” anafunsa mphunzitsiyo.

“Chifukwa bodza limakhalabe. Pamene 150,000 Kwacha zonse zatha, ndipo zinthu zomwe zinagulidwa zatha, BODZA limakhalabe chikhalire.

Choonadi ndi chofunika mokwanira kotero kuti ife tiyenera kulola kuwona zovuta chifukwa cha choonadi. Tikataya ungwiro wathu kuti tipewe kuchititsidwa manyazi nthawi ino, ndiye kuti tataya chinthu chopambana. Ndalama zopezeka mwa chinyengo ndi malipiro achabe, chifukwa cha chikumbumtima chodetse-dwa ndi chiweruzo chosatha chimene Mulungu amayika pa tchimo limeneli.

Kodi munganene kuti mukuyenda mu kuwunika kwa Mulungu pamene nthawi yomweyo mukuchita ntchito zoipa monga izi:

- Kusakhululukira abale kapena alongo?

- Kusakonzetsa zolakwika pamene munalakwira ena?

- Kuonjezera nkhani?

- Kuphwanya lonjezo?

- Kuba zake za Mulungu,chachikhumi ndi chopereka?

Kukhulupirika ndi yeso la chikhalidwe. Mulungu amadziwa mitima yathu, ndipo palibe chobisika ndi Iye. Komabe, nthawi zina sitikudziwonetsa kwa Mulungu monga m'mene amatidziwira ndi m'mene tikumvera m'kati mwa mitima yathu. Mwinanso sitimadziwonetsa kwa anthu ena m'mene ife tili. Munthu wa chisangalalo choona ndi iye amene amakhala wokhulupirika kwa Mulungu, ndipo amavomereza m'mene alili. Pamene tikutsegula mitima ndi miyoyo yathu kwa Mulungu mavuto awa angathe kutha.

Zolinga ndi chikhalidwe chathu ziyenera kuyesedwa ndi yeso la choonadi. Kuti tipambane yeso limeneli la zochita-chita zathu ndi Mulungu ndiponso anthu, tikusowa kusinthika m'kati mwathu chifukwa za kunja zimawonetsa za m'kati mwa munthu. Kodi inu ndi munthu wokhulupirika? Mulungu amafunitsitsa choonadi, dzikonso limachiyembekeza, ife tonse timapindula nacho. Ndi moyo wokhawo umene umapindula. “Pofuna kukhala nao makhalidwe abwino” (Ahebri 13:18). “Musabwezere munthu ali yense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pa maso pa anthu onse” (Aroma 12:17). Wereganinso Levitiko 19:35-36, (“Musamachita chisalungamo poweruza mlandu, poyesa utali wache, kulemera kwache, kapena kuchuruka kwache. Mukhala nacho choyesera choona, miyeso yoona, efa woona, hini woona; Ine ndine Yehova Mulungu wanu…”) ndiponso Miyambo 19:5, (“Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; Wolankhula mabodza sadzapulumuka”).

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.

Ndikadzafa, Chotsatira Ndi Chiyani?

Nthawi ino muli ndi moyo;mukupuma;mukudya ndi kumwa madzi tsiku ndi tsiku; mukutha kuyendayendakugwira ntchito zanu ndi kumagona. Mwina mukukhala moyo wokandwa mwina wodandaula chifukwa cha mabvuto. Tsiku ndi tsiku dzuŵa likutuluka ndipo likuloŵa; ku malo ena mwana akubadwa, komanso kumalo ena wina akumwalira.

PAMENEPA TIONA KUTI ZONSE ZA MOYO

WAPANSI PANO NDI ZOSAKHALITSA.

KOMA,

NDIKADZAFA NDIDZAPITA KUTI?

Kaya ndine Mkhristu wofooka

kapena wopembedza ku Chisilamu

kapena wopembedza ku Chibuda

kapena wopembedza ku Chiyuda

kapena wopembedza mizimu ya makolo

kapena wopembedza chimodzi cha zipembezo

zambiri zimene tingazitchule,

kapena wosapembedza kumene –

Koma tiyenera kuyankha funso lofunika kwambirili, chifukwa pakutha pa moyo wapansi pano, wa kanthawiwu, munthu ayenera kupita kwawo kumene kuli kokhalitsa.

NANGA KUMENEKU NDI KUTI?

Popeza kuti: Manda amene mudzakwiriridwamo sadzakwirira mzimu wanu, ngakhale mutadyedwa ndi chilombo kepena mbalame, sizidzameza mzimu wanu, kaya mudzamizidwa ndikufera mnyanja, mzimu wanu siudzamira mmadzimo,  ngakhale thupi lanu litatenthedwa ndi moto, mzimu wanu siungapsye.

MZIMU WANU SIUDZAFA!

Nkhani yonse ya: Ndikadzafa, Chotsatira Ndi Chiyani?

MULUMGU AMENE ANALENGA

KUMWAMBA NDI DZIKO LAPANSI

AKUTI, “MIZIMU YONSE NDI YANGA.”

Ku malo ena utatha moyo uno, “INUYO” mudzakomana ndi zones zimene munachita mdziko lapansi mmoyo wanu wathupi – zabwino kapena zoipa.

Tikhoza kumapembedza mokhulupirika.

Tikhoza kumva chisoni ndi zolakwa zathu.

Tikhoza kubwezera zimene tinaba.

Zoonadi zonsezi ndi zoyenera –

KOMA –

Sitingathe kudziyanjanitasa ndi Mulungu chifukwa cha zochimwa zathu. MULUNGU wakumwamba, woŵeruza  mwa chilungamo padziko lonse lapansi amadziŵa machismo anu ndi moyo wanu – palibe chobisika kwa Iye. Inu, ndi machismo anu simungathe kukaloŵa mu UFUMU ndi ULEMERERO wa dziko lirinkudza.

KOMA –

Mulungu wakumwambayu ndi Mulungu wachikondi. Iye wakonza njira yopulumutsira moyo ndi Mzimu wanu. Simudzaponyedwa ku chionongeko, kumoto, ngati mupemphera ndi kulapa machismo anu kwa Mulungu. Mulungu adzakukhululukirani kupyolera mwa Mwana wake Yesu Khristu. Yesu anazunzidwatu chifukwa cha zochimwa zanu, ngati mulambira ndi kupemphera kwa Iye yekha, adzalankhula za mtendere mmoyo wanu ndi kukupatsani moyo wa ulemerero mutafa pansi pano. Koma Yesuyo – amene ali Mwana wa Mulungu wamoyo, ayenera kukhala Mpulumutsi wanu choyamba. Mukatero ndiye kuti muli nacho chitsimikizo choti mudzakhala kudziko losatha, la chimwemwe chachikulu ndi mpumulo wa mzimu wanu. Koma HO!, dzenje la chionongeko ndi moto wosatha ziyembekezera iwo amene mmoyo uno akukana chikondi cha chipulumutso cha Ambuye Yesu. Sipadzakhalanso mwaŵi wolapa kapena kupulumuka mutafa. “Pamenepo idzauzanso a kudzanja lake lamanzere aja kuti, Chokani, inu anthu otembereredwa, Pitani kumoto wosatha umene Mulungu anaukonzera Satana ndi angelo ake” (Mateyu 25:41). “Ndipo wanychito wopanda pakeyu, mponyeni kunja kumdima, Kumeneko adzalira ndi kukukuta mano” (Marko 25:30). Mulungu, m’Buku Lopatulika, akuchenjezeratu mokwanira za chiŵeruzo chadziko lapansi chimene chiri pafupi. Mau a Mulungùŵa akuneneratu kuti lisanafike tsiku loyembekezeka la chiŵeruzolo padzakhala zizindikiro zoonekeratu zomwe zinanenedwa kale. Asanadze iye kudzakhala nkhondo ndi mbiri za nkhondo, kuukirana kwa mitundu, wina ndi unzake – sipadzakhalanso njira zakuthetsera kusiyana maganizo ndi kusamvana kwawo. Kudzakhala zibvomezi mmalo osiyanasiyana ndi milili ya matenda woopsya. Zonsezitu zakwanitsidwa kale mzaka zino. Mau a Mulungu aneneranso kuti anthu ochimwa adzachita zoipitsitsa ndipo sadzamvera chenjezo lirilonse, ndipo adzakonda chitayiko koposa Mulungu. Tikumbukire kuti Mfumu yathu yaikulu ndi ya chiŵeruzo cholungama siidzaganizira za kulemera kapena kusauka kwa munthu, kutchuka kwake kapena ulemu umene ali nawo, khungu kapena mtundu, kapena chipembedzo. Tsiku lina tidzaima osoŵa cholankhula pamaso pa Mlengi ndi Mfumu yathu, ngati tinyozera kubvomereza chipulumutso chimene watipatsa. Nthawi ya ulemerero wosatha imene ikubwerayo sikudzakhala kuŵerenga nthawi, masiku, nyengo kapena zaka. Utsi wa msautso wa anthu ochimwa ndi wokana Mulungu udzafuka nthawi zones osaleka – mmene nthawi yomweyo chimwemwe, mtendere, mpumulo ndi kuyimba kwa opulumutsidwa zidzakhalanso zosatha nthawi zones kumwambako. Dzisankhireni nokha nthawi ino! Ngati mukuganiza za nthawi ina, ndiye kuti mukuchedwa. Ŵerengani Uthenga Wabwino wa Mateyu, Marko, Luka ndi Yohane, mukatero ŵerengani Chipangano Chatsopano chonse. Kenako Buku Lopatulika lonse.

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.

Bwanji Za Mankhwala, Zoledzeretsa, Ndi Chiwerewere?

"Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa..." (Aroma 6:23)

Tiyeni tinene zoonadi. Zirombo zoopsya kumwa zoledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere ziri  nkuopsyeza ndiponso kuononga chimene Mulungu anachilenga kukhala chokoma ndiponso chabwino. Monga mchitidwe wa Octopus wamphamvuyo, izi zimakoka ang'ono komanso aakulu ndi kuwafumbatira.

Anthu ambiri amakakamizidwa pambali iliyonse ndi zokhumba zao, monga manyuzi pepala komanso ndi kuitanira kwa television. Maso ndi makutu zimalunjika kumene kuli zosokoneza zokhazokha zomwe zotsatira zake ndi kukhala ndi moyo wa uzimu komanso wa kuthupi wobwerera m'mbuyo. Temberero la chakumwa choledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere zaleka chitsanzo chokoma cha m’midzi yathu popanda kuongoledwa ndipo ziri nkupita ku chionongeko.

Kodi nanga ndi mbadwo wokha wa ana womwe utsutsidwe? Ayi. Naonso makolo ambiri asiyanso chikhalidwe chokoma, natsata chikhalidwe choipa, machismo ambiri ochitidwa ndi ana ambiri lero, makolo awo amangowalekerera osadziwa kuti alikupanga ana awo kuti adzakhale zidakwa, ogwiritsa ntchito mankhwala osaloledwa, ndi osuta pakulephera iwo kudzudzula pa kumwa zoledzeletsa ndi kusuta.

Mwadala, pakufuna kukhala osamvera malamulo olunjika a Mulungu makolo naonso ali pa njira yotsetsereka yopita ku mnyozo panopa komanso moyo ulinkudzawo. Kulira kopfuula kuyenera kukwera kumwamba. Tingadzipulumutse bwanji ife ndi ana athu?

M'manyumba mwathu, m'masukulu ndiponso m’makoleji sangathe kutulutsa chitsanzo chabwino choyenera nzika za dziko monga momwe maiko athu afunira ngati kumwa zoledzeretsa ndi kugwiritsa ntchito mankhwala zirigoyang'anidwa ndi kulimbikitsidwa ndi makolo opanda chikhalidwe chabwino, aphunzitsi ndi iwo anzeru zakuya . (Professors}, kuonongeka kwachikhalidwe chabwino m'masukulu kuli nkuopsezanso. Sipanathe zaka zambiri pamene aphunzitsi ndi anzeru zakuya akadachotsedwa ntchito chifukwa cholekerera ana asukulu kukhala ndi makhalidwe oipa.

Mliri umene watenga malo kwambiri mbadwo wathu uno ndi kumwa mwa uchidakwa kumenenso kumaononga chikhalidwe chabwino. Kuononga chikhalidwe ndi kumwaza ndalama pamene miyanda miyanda ya anthu alikusowa chakudya. Ichi ncha umphawi komanso chopereka magawano m'manyumba mwathu, ndiponso lonyoza dalitso loyera la Mulungu pa mtundu wa anthu.

Nkhani yonse ya: Bwanji Za Mankhwala, Zoledzeretsa, Ndi Chiwerewere?

Kuphatikiza kuipa kwa kumwa zoledzeretsa kwaonjezeranso kagwiritsidwe ka mankhwala osaloledwa. Kuipa kwa mankhwalawa kumaposa phindu lomwe mankhalawa amapereka. Kugwiritsa ntchito mankhwala osaloledwawa kungapangitsenso kuweruza molakwika ndiponso kuonongeka kwa nzeru. Ogwiritsa ntchito mankhwalawa naonso amabvomereza kuti ndi ulendo waku imfa mu nzeru, kuthupi lanyama, mu mzimu komanso kungathe kuononga ubongo. Kuphana ndi kudzipha ndizo zotsatira zake zoopsya za mchitidwe umenewu.

Khristu, m"Chipangano Chatsopano, anaika chitsanzo cha makhalidwe abwino. Naikanso ndime ya chikhalidwe chabwino. Mulungu analenga munthu kuti mtundu wa anthu uchuluke ndi kuti anthu adzikwatirana mwamuna ndi mkazi. lye anaikanso kuti padzikhala kufunana koyenera pa moyo Wa m’banja. Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; koma adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu. Aheb. 13:4

Anthu ambiri ali kuzunzika ndi miZimu ya chilakolako. Zotsatira zake zimakhala nkhondo yeniyeni pakati pa thupi ndi Mzimu. Thupi limafuna kukhala ndi ufulu wa kuchita zokondweretsa zake popanda choletsa, pamene Mzimu amadziwa bwino kuti malamulo onse a Mulungu ayenera kutsatidwa bwino. Chiwerewere sichingathe kuthetsa kutentha mtima kwa chilakolako, monganso mowa wa whisky umalephera kuchotsa ludzu la mowa. Apa choonadi ndiye chili pa mbali ina osati iyi ayi.

Chiwerewere, chigololo, dama la amunaokhaokha ndi chiwerewere china chirichonse pakati pa munthu ndi nyama ndi choletsedwa m'Mawu a Mulungu. Chiwerewere chimabweretsa kuwawa, kupweteka mtima, umphawi, kuchimwa, ndiponso kutenga matenda. Lev 18:23, Agalatiya 5.19-21. Chiyero chimabweretsa chisoni kuti anthu oyenera ndi olongosoka ali kukhala mu umphawi pamene munthu wopanda pache ali nazo zonse zomuyenereza. Mtumwi Paulo m'buku la Aroma akunena za momwe Mulungu adzaweruzire ochita chiwerewere cha amuna okhaokha. Chifukwa cha ichi, Mulungu nawapereka iwo ku zilakolako za manyazi: Pakuti ngakhale akazi awo anasandutsa machi- tidwe awo achibadwidwe kukhala osalingana ndi chibadwidwe: Chimodzimodzinso amuna, anasiya chikhalidwe cha chibadwidwe cha akazi, natenthetsana wina ndi mzake, amuna okhaokha ndi kuchita cbosayenera kuti akalandire mphoto yoywera m'chitidwe umenewu. Monga momwe iwo sanafuna kukhala naye Mulungu m'nzeru zao .. Mulungu anawapereka ku mtima wokanika, kuchita zosayenera: Pakudziwa chiweruzo cha Mulungu, kuti ochita zimenezi ayenera kufa, chifukwa samangodzichita kokha ayi, komanso amakondwera nazo. (Aroma 1:26,28,32). Ili linali tchimo lonyansa kwambiri la Sodomu ndi Gomora limene linabweretsa kulanga kwa Mulungu pakati pawo (Gen. 19). Monga mwa Malemba Oyera kuti nkovuta kuti Mzimu Woyera kubwereranso m 'mitima yathu ndi kukhal m'moyo wa Chikristu ngati tiri kukhala natichitabe machimo amenewa.

Mkati mwa chiwerewerechi ndi khungu la uzimu, la tchimo lomwe kuli kusowa manyazi pakusapembedza Mulungu, tiyenera kutembenukira ku Buku Lopatulika lomwe liri ndi udindo wonse wosakaikitsa wa muyaya pa chabwino kapena choipa.

Wokondedwa wowerengawe, kukhala ndi moyo wokondwa, ndi inuyo kukhala ndi mtendere ndi Mulungu, muyenera kudza m'chiyanjano pamodzi ndi lye.

Chigonjetso chiri kukuyembekezani! Muyenera kuzindikira ndi kulapa kuti muli ochimwa ndipo mukhulupilire kuti Yesu anafa pa mtanda atasenza tchimo lanu. Pamene mutsegula mtima wanu kwa Mulungu ndi kulapa machimo anu, lye adzakukhululukarani. Ngati tibvomereza machimo athu, lye ali wokhulupirika ndi wolungama kutikhululukira ife machismo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chirichonse.

Muyenera kupereka mtima wanu wonse kwa Yesu, Mpulumutsi wanu, ndipo tsatirani bwino pomvera Mau Ake ndi Mzimu Woyera. Madalitso a moyo wosinthika ndi maganizo oyera omwe amabweretsa kusinthika kotheratu m'zochita zanu. Khristu adzakulimbitsani mtima pokomana ndi mabvuto a moyo ndi mphamvu yogonjetsa mayesero omwe angakuzungu- lireni. ldzani kwa Yesu tsopano pamene mumva kuitana kwake. "Funani Yehova popezekalye, itanani lye pamene ali pafupi. ... "  (Yesaya 55:6).

Lumikizanani nafe.

Pezani mauthenga olembedwa.